Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 15:17-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Caka ca makumi atatu mphambu zisanu ndi zinai ca Azariya mfumu ya Yuda, Menahemu mwana wa Gadi analowa ufumu wace wa Israyeti, nakhala mfumu zaka khumi m'Samariya.

18. Nacita coipa pamaso pa Yehova masiku ace onse, osaleka zolakwa za Yerobiamu mwana wa Nebati, zimene analakwitsa nazo Israyeli.

19. Pamenepo Puli mfumu ya Asuri anadza kudzamenyana ndi dziko, koma Menahemu anampatsa Puli matalente a siliva cikwi cimodzi; kuti dzanja lace likhale naye kukhazikitsa ufumu m'dzanja lace.

20. Ndipo Menahemu anasonkhetsa Israyeli ndaramazi, nasonkhetsa acuma, yense masekeli makumi asanu a siliva: kuti azipereke kwa mfumu ya Asuri. Nabwerera mfumu ya Asuri osakhala m'dzikomo.

21. Macitidwe ena tsono a Menahemu, ndi zonse anazicita, sizinalembedwa kodi m'buku la macitidwe a mafumu a Israyeli?

22. Nagona Menahemu ndi makolo ace; nakhala mfumu m'malo mwace Pekahiya mwana wace.

23. Caka ca makumi asanu a Azariya mfumu ya Yuda, Pekahiya mwana wa Menahemu analowa ufumu wace wa Israyeli m'Samariya, nakhala mfumu zaka ziwiri.

24. Nacita coipa pamaso pa Yehova, sanaleka zolakwa za Yerobiamu mwana wa Nebati, zimene analakwitsa nazo Israyeli.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 15