Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 15:13-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Salumu mwana wa Yabesi analowa ufumu wace caka ca makumi atatu mphambu zisanu ndi zinai ca Uziya mfumu ya Yuda, nakhala mfumu mwezi umodzi m'Samariya.

14. Koma anakwera Menahemu mwana wa Gadi kucokera ku Tiriza, nafika ku Samariya, nakantha Salumu mwana wa Yabesi m'Samariya, namupha; nakhala mfumu m'malo mwace.

15. Macitidwe ena tsono a Salumu ndi ciwembu cace anacicita, taonani, zalembedwa m'buku la macitidwe a mafumu a Israyeli.

16. Pamenepo Menahemu anakantha Tifisa, ndi onse anali m'mwemo, ndi malire ace kuyambira ku Tiriza; popeza sanamtsegulira pacipata; anaukantha, natumbula akazi onse a pakati okhala m'mwemo.

17. Caka ca makumi atatu mphambu zisanu ndi zinai ca Azariya mfumu ya Yuda, Menahemu mwana wa Gadi analowa ufumu wace wa Israyeti, nakhala mfumu zaka khumi m'Samariya.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 15