Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 14:18-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Macitidwe ena tsono a Amaziya, kodi sizilembedwa m'buku la macitidwe a mafumu a Yuda?

19. Ndipo anamcitira ciwembu m'Yerusalemu, nathawira iye ku Lakisi; koma anatumiza akumtsata ku Lakisi, namupha komweko.

20. Nabwera naye pa akavalo, namuika ku Yerusalemu pamodzi ndi makolo ace m'mudzi wa Davide.

21. Ndipo anthu onse a Yuda anatenga Azariya, (ndiye Uziya), ndiye wa zaka khumi mphambu zisanu ndi cimodzi, namlonga ufumu m'malo mwa atate wace Amaziya,

22. Anamanga Elati, naubweza kwa Yuda, atagona ndi makolo ace mfumuyo.

23. Caka cakhumi ndi zisanu ca Amaziya mwana wa Yoasi mfumu ya Yuda, Yerobiamu mwana wa Yoasi mfumu ya Israyeli analowa ufumu wace m'Samariya, nakhala mfumu zaka makumi anai mphambu cimodzi.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 14