Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 1:7-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ndipo iye ananena nayo, Nanga maonekedwe ace a munthu anakwerayo kukomana nanu, nanena nanu mau awa, ndi otani?

8. Ninena naye, Ndiye munthu wobvala zaubweya, namangira m'cuuno mwace ndi lamba lacikopa. Nati iye, Ndiye Eliya wa ku Tisibe.

9. Pamenepo mfumu inatuma kwa iye asilikari makumi asanu ndi mtsogoleri wao. Iye nakwera kumka kwa Eliya; ndipo taonani, analikukhala pamwamba pa phiri. Ndipo analankhula naye, Munthu wa Mulungu iwe, mfumu ikuti, Tsika.

10. Nayankha Eliya, nanena ndi mtsogoleriyo, Ndikakhala ine munthu wa Mulungu, utsike mota wakumwamba, nunyeketse iwe ndi makumi asanu ako. Pamenepo unatsika mota kumwamba, nunyeketsa iye ndi makumi asanu ace.

11. Ndipo anabwereza kutuma kwa iye mtsogoleri wina ndi makumi asanu ace. Ndipo iye anayankha nanena naye, Munthu wa Mulungu iwe, itero mfumu, Tsika msanga.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 1