Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 9:1-2 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo panali munthu Mbenlamlni, dzina lace ndiye Kisi, mwana wa Abiyeli, mwana wa Zerori, mwana wa Bekorati, mwana wa Afiya, mwana wa Mbenjamini, ndiye ngwazi.

2. Iye anali ndi mwana wamwamuna dzina lace Sauli, mnyamata wokongola; pakati pa anthu onse a Israyeli panalibe wina wokongola ngati iye; anali wamtali, anthu onse ena anamlekeza m'cifuwa.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 9