Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 6:14-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Ndipo garetalo linafika m'munda wa Yoswa wa ku Betisemesi, ndi kuima momwemo, pa mwala waukuru; ndipo anawaza matabwa a garetalo, nazipereka ng'ombezo nsembe yopsereza kwa Yehova.

15. Ndipo Alevi anatsitsa likasa la Yehova, ndi bokosi linali nalo, m'mene munali zokometsera zagolidi, naziika pa mwala waukuruwo; ndipo anthu a ku Betisemesi anapereka nsembe zopsereza, naphera nsembe kwa Yehova tsiku lomwelo.

16. Ndipo pamene mafumu asanu a Afilisti anaonerako, anabwerera kunka ku Ekroni tsiku lomwelo.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 6