Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 5:10-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Cifukwa cace anatumiza likasa la Mulungu ku Ekroni. Ndipo kunali pofika likasalo ku Ekroni, a ku Ekroni anapfuula nati, Anadzatitulira likasa la Mulungu wa Israyeli, kutipha ife ndi ana athu.

11. Cifukwa cace anatumiza, nasonkhanitsa mafumu onse a Afilisti, ndipo iwowa anati, Cotsani likasa la Mulungu wa Israyeli, lipitenso kumalo kwace, kuti lingationonge ife, ndi anthu athu; pakuti kunali kusautsa koopsa m'mudzi monse; dzanja la Mulungu linabvutadi pamenepo.

12. Ndipo amene anapanda kufa anagwidwa ndi mafundowo; ndi kulira kwa mudziwo kunakwera kumwamba.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 5