Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 26:23-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Ndipo Yehova adzabwezera munthu yense cilungamo cace ndi cikhulupiriko cace, popeza Yehova anakuperekani lero m'dzanja langa, koma sindinalola kutukulira dzanja langa pa wodzozedwa wa Yehova,

24. Ndipo onani, monga lero ndinasamalira ndithu moyo wanu, momwemo usamaliridwe ndithu moyo wanga pamaso pa Yehova, ndipo iye andipulumutse ku masautso onse.

25. Pomwepo Sauli anati kwa Davide, Udalitsike iwe, mwana wanga Davide; udzacita ndithu camphamvu, nudzapambana. Comweco Davide anamuka, ndipo Sauli anabwera kwao.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 26