Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 25:9-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Ndipo pakufika anyamata a Davide, analankhula ndi Nabala monga mau aja onse m'dzina la Davide, naleka.

10. Koma Nabala anayankha anyamata a Davide nati, Davide ndani? ndi mwana walese ndani? Makono ano pali anyamata ambiri akungotaya ambuye ao.

11. Kodi ndidzatenga mkate wanga, ndi madzi anga, ndi nyama imene ndinaphera osenga nkhosa anga, ndi kuzipatsa anthu amene sindidziwa kumene afumira?

12. Comweco anyamata a Davide anatembenukira ku njira yao, nabwerera, nadza namuuza monga mwa mau onse awa.

13. Ndipo Davide anati kwa anthu ace, Munthu yense wa inu amangirire lupanga lace. Namangirira munthu yense lupanga lace; ndi Davide yemwe anamangirira lupanga lace; ndipo anakwera kumtsata Davide monga anthu mazana anai, koma mazana awiri anadika akatundu.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 25