Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 20:34-39 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

34. Pamenepo Jonatani anauka pagome wolunda ndithu, osadya kanthu tsiku laciwiri la mwezi, pakuti mtima wace unali ndi cisoni cifukwa ca Davide, popeza atate wace anamcititsa manyazi.

35. Ndipo m'mawa, Jonatani ananka kuthengoko pa nthawi imene anapangana ndi Davide, ali ndi kamnayamata.

36. Ndipo anauza mnyamata waceyo, Thamanga uzikatola mibvi Imene ndidzaponya; ndipo analikuthamanga mnyamatayu, iye anaponya mubvi kuutumphitsa iye.

37. Ndipo mnyamatayo atafika pa malo a mubvi umene Jonatani anauponya, Jonatani anapfuulira mnyamatayo, nati, Mubviwo suli m'tsogolo mwako kodi?

38. Ndipo Jonatani anapfuulira mnyamatayo, nati, Yendesa, fulumira, usaima. Ndi mnyamata wa Jonatani anatola mibvi, nafika kwa mbuye wace.

39. Koma mnyamatayo sanadziwa kanthu; Davide ndi Jonatani okha anadziwa za mranduwoo.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 20