Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 20:19-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Ndipo atapita masiku atatu, utsike msanga, nufike kumene unabisala tsiku la mrandu uja, nukhale pa mwala wa Ezeri.

20. Ndipo ine ndidzaponya mibvi itatu pambali pace, monga ngati ndirikuponya pacandamali.

21. Ndipo taona, ndidzatumiza mnyamatayo, ndi kuti, Kafune mibviyo, Ndikamuuza mwanayo, kuti, Taona mibvi iri cakuno; uitole nubwere, popeza pali mtendere kwa iwe, palibe kanthu, pali Yehova.

22. Koma ndikati kwa mnyamatayo, Ona mibvi iri kutsogoloko; pamenepo unyamuke ulendo wako; popeza Yehova wakuuza umuke.

23. Ndipo za cija tinakambirana iwe ndi ine, taona, Yehova ali pakati pa ife nthawi zonse.

24. Comweco Davide anabisala kuthengo; ndipo pakukhala mwezi, mfumu inakhala pansi kudya.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 20