Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 2:8-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Amuutsa waumphawi m'pfumbi,Nanyamula wosowa padzala,Kukamkhalitsa kwa akalonga;Ndi kuti akhale naco colowa ca cimpando ca ulemerero;Cifukwa nsanamira za dziko lapansi nza Yehova,Ndipo iye anakhazika dziko pa izo,

9. Adzasunga mapazi a okoodedwaace,Koma oipawo adzawakhalitsa cete mumdima;Pakuti palibe munthu adzapambana ndi mphamvu,

10. Otsutsana ndi Yehova adzaphwanyika;Kumwamba iye adzagunda pa iwo:Yehova adzaweruza malekezero a dziko:Ndipo adzapatsa mphamvu mfumuyace,Nadzakweza nyanga ya wodzozedwa wace.

11. Ndipo Elikana anauka kwao ku Rama, mwanayo natumikira Yehova pamaso pa Eli wansembeyo.

12. Koma ana a Eli anali oipa; sanadziwa Yehova.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 2