Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 2:24-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Iai, ana anga, popeza mbiri imene ndirikuimva siri yabwino iai; mulikulakwitsa anthu a Yehova.

25. Munthu akacimwira munthu mnzace oweruza adzaweruza mrandu wace; koma ngati munthu acimwira Yehova, adzampembedzera ndani? Koma ngakhale adatero, iwo aja anakhalabe osamvera mau a atate wao, cifukwa Yehova adati adzawaononga.

26. Ndipo mwanayo Samueli anakulakula, ndipo Yehova ndi anthu omwe anamkomera mtima.

27. Ndipo anafika kwa Eli munthu wa Mulungu, nanena naye, Atero Yehova, Kodi Ine ndinadziulula kwa banja la kholo lako, muja anali m'Aigupto, m'nyumba ya Farao?

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 2