Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 18:28-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

28. Ndipo Sauli anaona, nadziwa kuti Yehova ali ndi Davide; ndi kuti Mikala mwana wa Sauli anamkonda Davide.

29. Sauli nayamba kumuopa Davide kopambana; ndi Sauli anali mdani wa Davide masiku onse.

30. Pomwepo mafumu a Afilisti anaturuka; ndipo nthawi zonse anaturuka iwo, Davide anali wocenjera koposa anyamata onse a Sauli, comweco dzina lace linatamidwa kwambiri.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 18