Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 17:12-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Tsono Davide anali mwana wa M-efrati uja wa ku Betelehemu-Yuda, dzina lace ndiye Jese; ameneyu anali nao ana amuna asanu ndi atatu; ndipo m'masiku a Sauli munthuyo anali nkhalamba, mwa anthu.

13. Ndipo ana atatu akuru a Jese anatsata Sauli kunkhondoko; ndi maina ao a ana ace atatuwo adapita ku nkhondowo ndiwo Eliabu woyambayo, ndi mnzace womponda pamutu pace Abinadabu, ndi wacitatu Sama.

14. Ndipo Davide anali wotsiriza; ndi akuru atatuwo anamtsata Sauli.

15. Koma Davide akamuka kwa Sauli, nabwerera kudzadyetsa nkhosa za atate wace ku Betelehemu.

16. Ndipo Mfilistiyo anayandikira m'mawa ndi madzulo, nadzionetsera masiku makumi anai.

17. Ndipo Jese anati kwa Davide mwana wace, Uwatengere abale ako efa watirigu uyu wokazinga, ndi mikate iyi khumi, nuthamangire nazo kuzithando kwa abale ako;

18. nunyamule ncinci izi khumi zamase ukapatse mtsogoleri wa cikwi cao, nukaone m'mene akhalira abale ako, nulandire cikole cao,

19. Tsono Sauli, ndi iwowa, ndi anthu onse a Israyeli, anali m'cigwa ca Ela, ku nkhondo ya Afilisti.

20. Ndipo Davide anauka m'mamawa, nasiyira nkhosa wozisungira, nasenza zija, namuka, monga anamuuza Jese; ndipo iye anafika ku linga la magareta, napeza khamu lirikuturuka kunka poponyanira nkhondo lirikupfuula.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 17