Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 16:6-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ndipo kunali, pakufika iwo, iye anayang'ana pa Eliyabu, nati, Zoonadi, wodzozedwa wa Yehova ali pamaso pace.

7. Koma Yehova ananena ndi Samueli, Vsayang'ane nkhope yace, kapena kutalika kwa msinkhu wace, popeza Ine ndinamkana iye; pakuti Yehova saona monga aona munthu; pakuti munthu ayang'ana cooneka ndi maso, koma Yehova ayang'ana mumtima.

8. Pamenepo Jese anaitana Abinadabu nampititsa pa Samueli. Ndipo iye adati, Koma uyunso Yehova sadamsankha.

9. Pamenepo Jese anapititsapo Sama. Ndipo anati, Koma uyunso Yehova sanamsankha.

10. Ndipo Jese anapititsapo ana ace amuna asanu ndi awiri. Koma Samueli anati kwa Jese, Yehova sanawasankha awa.

11. Ndipo Samueli anati kwa Jese, Ana anu ndi omwewa kodi? Nati iye, Watsala wina, mng'ono wa onse, ndipo taonani, iye alikuweta nkhosa. Ndipo Samueli anati kwa Jese, Tumiza munthu akamtenge; pakuti ife sitidzakhala pansi kufikira iye atadza kuno.

12. Ndipo anatumiza munthu, nabwera naye. Tsono iye anali wofiirira, ndi wa nkhope yokongola, ndi maonekedwe okoma. Ndipo Yehova anati, Nyamuka umdzoze, pakuti ndi ameneyu.

13. Pamenepo Samueli anatenga nyanga ya mafuta, namdzoza pakati pa abale ace; ndipo mzimu wa Yehova unalimbika pa Davide kuyambira tsiku lomweli. Ndipo Samueli ananyamuka, Danks ku Rama.

14. Koma mzimu wa Yehova unamcokera Sauli, ndi mzimu woipa wocokera kwa Yehova unambvuta iye.

15. Ndipo anyamata a Sauli ananena naye, Onani tsopano, mzimu woipa wocokera kwa Mulungu ulikubvuta inu.

16. Tsono inu mbuye wathu muuze anyamata anu, amene ali pamaso panu, kuti afune munthu wanthetemya wodziwa kuyimba zeze; ndipo kudzakhala, pamene mzimu woipa wocokera kwa Mulungu uli pa inu, iyeyo adzayimba ndi dzanja lace, ndipo mudzakhala wolama.

17. Ndipo Sauli anati kwa anyamata ace, Mundifunire tsono munthu wakudziwa kuyimba bwino, nimubwere naye kwa ine.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 16