Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 15:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Samueli ananena ndi Sauli, Yehova ananditumiza ine kukudzozani mukhale mfumu ya anthu ace Aisrayeli; cifukwa cace tsono mumvere kunena kwa mau a Yehova.

2. Atero Yehova wa makamu, Ndinaonerera cimene Amaleki anacitira Israyeli, umo anamlalira panjira, m'mene iye anakwera kuturuka m'Aigupto.

3. Muka tsopano, nukanthe Amaleki, nuononge konse konse zonse ali nazo, usawalekerere, koma uwaphe mwamuna ndi mkazi, mwana ndi woyamwa, ng'ombe ndi nkhosa, ngamila ndi buru.

4. Ndipo Sauli anamemeza anthu, nawawerenga ku Telayimu, akuyenda pansi zikwi mazana awiri, ndi a kwa Yuda anthu zikwi khumi.

5. Ndipo Sauli anafika ku mudzi wa Amaleki, nalalira kucigwa.

6. Ndipo Sauli anauza Akeni kuti, Mukani, cokani mutsike kuturuka pakati pa Aamaleki, kuti ndingakuonongeni pamodzi ndi iwo; pakuti inu munacitira ana a Israyeli onse zabwino, pakufuma iwo ku Aigupto. Comwece Akeni anacoka pakati pa Aamaleki.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 15