Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 14:46-52 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

46. ndi Afilistiwo anamuka ku malo a iwo okha.

47. Ndipo pamene Sauli atakhazikitsa ufumu wa pa Israyeli, iye anaponyana ndi adani ace onse pozungulira ponse, ndi Moabu, ndi ana a Amoni, ndi Edomu ndi mafumu a Zoba, ndi Afilisti; ndipo pali ponse anapotolokerapo, anawalanga.

48. Ndipo iye anakula mphamvu, nakantha Aamaleki, napulumutsa Aisrayeli m'manja a akuwawawanya.

49. Ndipo ana a Sauli ndiwo Jonatani, ndi Isivi, ndi Malikisuwa; ndi maina a ana akazi ace awm ndi awa: dzina la woyamba ndiye Merabu, ndi dzina la mng'ono wace ndiye Mikala;

50. ndi dzina la mkazi wa Sauli ndi Ahinamu mwana wa Ahimazi; ndi dzina la kazembe wa khamu lankhondo lace ndiye Abineri mwana wa Neri, mbale wace wa atate wa Sauli.

51. Ndipo atate wa Sauli ndiye Kisi; ndipo Neri atate wa Abineri ndiye mwana wa Abiyeli.

52. Ndipo panali nkhondo yowawa ndi Afilisti masiku onse a Sauli; ndipo Sauli pakuona munthu wamphamvu, kapena ngwazi, anamtenga akhale naye.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 14