Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 14:3-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. ndi Ahiya mwana wa Ahitubi mbale wace wa Ikabodi, mwana wa Pinehasi, mwana wa Eli, wansembe wa Yehova wa ku Silo, wobvala efodi. Ndipo anthuwo sanadziwa kuti Jonatani wacoka.

4. Ndipo pakati pa mipata imene Jonatani anafuna kupitapo kunka ku kaboma ka Afilisti, panali phiri lathanthwe pa mbali yina, ndi phiri lathanthwe pa mbali inzace; ndipo dzina la linalo ndilo Bozezi, ndi la linzace ndilo Sene.

5. Phiri lija linaimirira kuyang'ana kumpoto pandunji pa Mikimasi, ndi linzace kumwera pandunji pa Geba.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 14