Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 13:7-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ndipo Ahebri ena anaoloka Yordano nafika ku dziko la Gadi ndi Gileadi; koma Sauli akali ku Giligala, ndipo anthu onse anamtsata ndi kunthunthumira.

8. Ndipo iye anatsotsa masiku asanu ndi awiri, monga nthawi anampanga Samueli; koma Samueli sanafika ku Giligala, ndipo anthu anabalalika namsiya Sauli.

9. Pamenepo Sauli anati, Andipatsire kuno nsembe yopsereza, ndi nsembe zoyamika. Ndipo iye anapereka nsembe yopserezayo.

10. Ndipo kunali kuti pakutsiriza iye kupereka nsembe yopserezayo, pomwepo, onani, Samueli anafika. Ndipo Sauli anamcingamira kukamlankhula iye.

11. Ndipo Samueli anati, Mwacitanji? Nati Sauli, Cifukwa ndinaona kuti anthuwo alinkubalalika kundisiya ine, ndi kuti inu simunafika masiku aja tinapangana, ndi kuti Afilisti anasonkhana ku Mikimasi;

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 13