Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 11:10-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Cifukwa cace anthu a ku Yabezi anati, Mawa tidzaturukira kwa inu, ndipo mudzaticitira cokomera inu.

11. Ndipo m'mawa mwace Sauli anagawa anthu magulu atatu; ndipo iwowa anafika pakati pa zithandozo m'ulonda wa mamawa, nakantha Aamoni kufikira kutentha kwa dzuwa. Ndipo otsalawo anabalalika, osatsala pamodzi ngakhale awiri.

12. Ndipo anthu anati kwa Samueli, Ndani iye amene anati, Kodi Sauli adzatiweruza ife? tengani anthuwo kuti tiwaphe.

13. Koma Sauli anati, Sadzaphedwa lero munthu; pakuti lero Yehova anacita cipulumutso m'lsrayeli.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 11