Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mbiri 19:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo zitatha izi, Nahasi mfumu ya ana a Amoni anamwalira, ndi mwana wace anakhala mfumu m'malo mwace.

2. Ndipo Davide anati, Ndidzamcitira zokoma mtima Hanuni mwana wa Nahasi, popeza atate wace anandicitira ine zokoma mtima. Momwemo Davide anatuma mithenga imtonthoze mtima pa atate wace. Pofika anyamata ace a Davide ku dziko la ana a Amoni kwa Hanuni kumtonthoza mtima,

3. akalonga a ana a Amoni anati kwa Hanuni, Davide ali kucitira atate wanu ulemu kodi, popeza anakutumizirani otonthoza? sakudzerani kodi anyamata ace kufunafuna, ndi kugubuduza, ndi kuzonda dziko?

4. Ndipo Hanuni anatenga anyamata a Davide, nawameta, nadula malaya ao pakati kufikira m'matako, nawaleka acoke.

Werengani mutu wathunthu 1 Mbiri 19