Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 9:26-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Ndipo mfumu Solomo anamanga zombo zambiri ku Ezioni Geberi uli pafupi ndi Eloti, pambali pa Nyanja Yofiira, ku dziko la Edomu.

27. Ndipo, Hiramu anatuma anyamata ace m'zombozo amarinyero ozerewera m'nyanja, pamodzi ndi anyamata a Solomo.

28. Ndipo iwo anafika ku Ofiri, natengako golidi matalenti mazana anai mphambu makumi awiri, nafika naye kwa mfumu Solomo.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 9