Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 7:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Koma nyumba ya iye yekha Solomo anaimanga zaka khumi mphambu zitatu, natsiriza nyumba yace yonse.

2. Anamanganso nyumba yochedwa Nkhalango ya Lebano, m'litali mwace munali mikono zana limodzi, kupingasa kwace mikono makumi asanu, ndi msinkhu wace mikono makumi atatu; naisanja pa mizere inai ya mapanda amkungudza, ndi mitanda yamkungudza yotanthalika mapandawo.

3. Ndipo inayalidwa ndi mkungudza pamwamba pa zipinda makumi anai mphambu zisanu zolongosoledwa pa mapanda, mzere umodzi zipinda khumi mphambu asanu.

4. Ndipo panali mazenera m'mizere itatuyo, zenera limodzi lopenyana ndi linzace mizere itatu.

5. Ndipo makomo onse ndi mphuthu zonse zinali zamphwamphwa maonekedwe ace, ndipo zenera limodzi linapenyana ndi linzace mizere Itatu.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 7