Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 6:12-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Kunena za nyumba yino ulikuimanga, ukamayenda iwe m'malemba anga, ndi kumacita maweruzo anga, ndi kumasunga malamulo anga onse kuyendamo, pamenepo Ine ndidzakhazikitsira iwe mau anga amene ndinauza Davide atate wako.

13. Ndipo ndidzakhala pakati pa ana a Israyeli osawasiya anthu anga a Israyeli.

14. Tsono Solomo anamanga nyumbayo naitsiriza.

15. Ndipo anacinga makoma a nyumba m'katimo ndi matabwa amkungudza, kuyambira pansi kufikira posanja, nacinga m'katimo ndi matabwa, nayala pansi m'nyumbamo matabwa amlombwa.

16. Ndipo anadulitsa ndi matabwa amkungudza mikono makumi awiri m'kati mwa nyumba m'tsogolo mwace, kuyambira pansi kulekeza kumitanda; ici anamanga m'katimo cikhale monenera, malo opatulikitsa.

17. Ndipo nyumbayo, ndiyo Kacisi wa cakuno ca monenera, inali ya mikono makumi anai.

18. Ndipo m'kati mwa nyumba munali mikungudza yosemasema, ngati zikho ndi maluwa oti gada; munali mikungudza yokha yokha simunaoneka mwala ai,

19. Ndipo anakonza monenera m'kati mwa nyumba m'tsogolo mwace, kuikamo likasa la cipangano la Yehova.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 6