Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 6:10-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndipo anamanga zipindazo zogundana ndi nyumba yonseyo, cipinda ciri conse msinkhu wace mikono isanu; ndipo anazilumikizitsa kunyumba ndi mitengo yamkungudza.

11. Ndipo mau a Yehova anafika kwa Solomo, nati,

12. Kunena za nyumba yino ulikuimanga, ukamayenda iwe m'malemba anga, ndi kumacita maweruzo anga, ndi kumasunga malamulo anga onse kuyendamo, pamenepo Ine ndidzakhazikitsira iwe mau anga amene ndinauza Davide atate wako.

13. Ndipo ndidzakhala pakati pa ana a Israyeli osawasiya anthu anga a Israyeli.

14. Tsono Solomo anamanga nyumbayo naitsiriza.

15. Ndipo anacinga makoma a nyumba m'katimo ndi matabwa amkungudza, kuyambira pansi kufikira posanja, nacinga m'katimo ndi matabwa, nayala pansi m'nyumbamo matabwa amlombwa.

16. Ndipo anadulitsa ndi matabwa amkungudza mikono makumi awiri m'kati mwa nyumba m'tsogolo mwace, kuyambira pansi kulekeza kumitanda; ici anamanga m'katimo cikhale monenera, malo opatulikitsa.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 6