Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 22:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Aaramu ndi Aisrayeli anakhala cete zaka zitatu, osathirana nkhondo.

2. Koma kunacitika caka cacitatu, kuti Yehosafati mfumu ya Yuda anatsikira kwa mfumu ya Israyeli.

3. Ndipo mfumu ya Israyeli ananena ndi anyamata ace, nati, Kodi simudziwa kuti Ramoti Gileadi ngwathu, ndipo tangokhala cete, osaulanditsa m'dzanja la mfumu ya Aramu.

4. Tsono anati kwa Yehosafati, Kodi udzapita nane kunkhondo ku Ramoti Gileadi? Ndipo Yehosafati anati kwa mfumu ya Israyeli, M'mene ukhalira iwe ndi momwe ndikhalira ndine; anthu anga monga anthu ako, akavalo anga monga akavale ako.

5. Ndipo Yehosafati ananena ndi mfumu ya Israyeli, Fuusira ku mau a Yehova lero.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 22