Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 2:14-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Anatinso, Ndiri nanu mau, Nati iye, Tanena.

15. Nati iye, Mudziwa kuti ufumu unali wanga, ndi kuti Aisrayeli onse anaika maso ao pa ine, kuti ndikhale mfumu ndine; koma ufumu watembenuka nukhala wa mbale wanga, popeza iye anaulandira kwa Mulungu.

16. Ndipo tsopano, ndikupemphani pempho limodzi, musandikaniza. Ndipo mkaziyo anati kwa iye, Tanena.

17. Nati iye, Mundinenere kwa mfumu Solomo, popeza sakukanizani, kuti andipatse Abisagi wa ku Sunamu akhale mkazi wanga.

18. Ndipo Batiseba anati, Cabwino, ndidzakunenera kwa mfumu.

19. Tsono Batiseba ananka kwa mfumu Solomo kukanenera Adoniya kwa iye. Ndipo mfumu inanyamuka kukomana naye, namuweramira nakhalanso pa mpando wace wacifumu, naikitsa mpando wina wa amace wa mfumu, nakhala iye ku dzanja lace lamanja.

20. Pamenepo mkaziyo anati, Ndikupemphani kapempho kamodzi, musandikaniza. Ndipo mfumu inati kwa iye, Tapemphani amai wanga, popeza sindikukanizani.

21. Ndipo iye anati, Abisagi wa ku Sunamu apatsidwe kwa Adoniya mbale wanu akhale mkazi wace.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 2