Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 19:16-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. ukadzozenso Yehu mwana wa Nimsi akhale mfumu ya Israyeli; ukadzozenso Elisa mwana wa Safati wa ku Abelimehola akhale mneneri m'malo mwako.

17. Ndipo kudzacitika Yehu adzamupha amene adzapulumuka ku lupanga la Hazaeli; ndi Elisa adzamupha amene adzapulumuka ku lupanga la Yehu,

18. Ndiponso ndidasiya m'lsrayeli anthu zikwi zisanu ndi ziwiri osagwadira Baala maondo ao, osampso-mpsona ndi milomo yao.

19. Tsono anacokako, napeza Elisa mwana wa Safati alikukoketsa cikhasu ng'ombe ziwiri ziwiri magori khumi ndi awiri, iye yekha anakhala pa gori lakhumi ndi ciwiri; ndipo Eliya anamka kunali iyeyo, naponya copfunda cace pa iye.

20. Ndipo iye anasiya ng'ombe zija, namthamangira Eliya, nati, Ndiloleni ndithange ndakapsompsona atate wanga ndi amai wanga; nditatero ndidzakutsatani. Nati iye, Bwerera, ndakucitanji?

21. Ndipo anabwerera panali iye uja, natengako ng'ombe ziwiri, nazipha, naphikira nyama yace ndi zipangizo za zocitira nazo ng'ombe, napatsa anthu adye. Atatero, ananyamuka, natsata Eliya, namtumikira.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 19