Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 16:27-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Ndipo macitidwe ena a Omri anawacita, ndi mphamvu yace anaionetsa, kodi sizilembedwa m'buku la macitidwe a mafumu a Israyeli?

28. Nagona Omri ndi makolo ace, naikidwa m'Samaria; ndipo Ahabu mwana wace analowa ufumu m'malo mwace.

29. Ndipo caka ca makumi atatu mphambu zisanu ndi zitatu ca Asa mfumu ya Yuda Ahabu mwana wa Omri analowa ufumu wa Israyeli, nakhala Ahabu mwana wa Omri mfumu ya Israyeli m'Samaria zaka makumi awiri mphambu ziwiri.

30. Ndipo Ahabu mwana wa Omri anacimwa pamaso pa Yehova koposa onse adamtsogolerawo.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 16