Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 16:20-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Macitidwe ena tsono a Zimri, ndi ciwembu anacicitaco, kodi sizilembedwa m'buku la macitidwe a mafumu a Israyeli?

21. Pamenepo anthu a Israyeli anagawika pakati, anthu ena anatsata Tibini mwana wa Ginati kumlonga ufumu, ena natsata Omri.

22. Koma anthu akutsata Omri anapambana iwo akutsata Tibini mwana wa Ginati; nafa Tibini, Omri nakhala mfumu.

23. Caka ca makumi atatu ndi cimodzi ca Asa mfumu ya Yuda, Omri anayamba kukhala mfumu ya Israyeli, nakhala zaka khumi ndi ziwiri; ku Tiriza anali mfumu zaka zisanu ndi cimodzi.

24. Ndipo anagula kwa Semeri citunda ca Samaria ndi matalente awiri a siliva, namanga pacitundapo, nacha dzina lace la mudzi anaumanga Samaria, monga mwa dzina la Semeri mwini citundaco.

25. Koma Omri anacimwa pamaso pa Yehova, nacita zoipa koposa onse adamtsogolerawo.

26. Nayenda m'njira yonse ya Yerobiamu mwana wa Nebati, ndi chimo lace anacimwitsa nalo Aisrayeli, kuputa mkwiyo wa Yehova Mulungu wa Israyeli ndi zacabe zao.

27. Ndipo macitidwe ena a Omri anawacita, ndi mphamvu yace anaionetsa, kodi sizilembedwa m'buku la macitidwe a mafumu a Israyeli?

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 16