Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 15:29-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

29. Tsonokunacitika, pokhalamfumu iye, anakantha nyumba yonse ya Yerobiamu, osasiyako wamoyo ndi mmodzi yense wa Yerobiamu, kufikira adamuononga monga mwa mau a Yehova, amene analankhula pa dzanja la mtumiki wace Ahiya wa ku Silo;

30. cifukwa ca macimo a Yerobiamu, amene adacimwa nao, nacimwitsa nao Aisrayeli, ndi kuutsa kwace kumene anaputa nako mkwiyo wa Yehova Mulungu wa Israyeli.

31. Ndipo macitidwe ena a Nadabu, ndi zonse anazicita, kodi sizilembedwa m'buku la macitidwe a mafumu a Israyeli?

32. Ndipo panali nkhondo pakati pa Asa ndi Basa mfumu ya Israyeli masiku ao onse.

33. Tsono Basa mwana wa Ahiya analowa ufumu wa Israyeli caka cacitatu ca Asa mfumu ya Yuda, nakhala mfumu ku Tiriza zaka makomi awiri mphambu zinai.

34. Ndipo anacimwa pamaso pa Yehova, nayenda m'njira ya Yerobiamu, ndi m'chimo lace iye anacimwitsa nalo Israyeli.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 15