Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 14:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Nthawi yomweyo Abiya mwana wa Yerobiamu anadwala.

2. Ndipo Yerobiamu ananena ndi mkazi wace, Unyamuke, nudzizimbaitse, ungadziwike kuti ndiwe mkazi wa Yerobiamu, nupite ku Silo; taona, kumeneko kuli Ahiya mneneri uja anandiuza ine ndidzakhala mfumu ya anthu awa.

3. Nupite nayo mikate khumi, ndi timitanda, ndi cigulu ca uci, numuke kwa iye; adzakuuza m'mene umo akhalire mwanayo.

4. Natero mkazi wa Yerobiamu, nanyamuka namka ku Silo, nalowa m'nyumba ya Ahiya. Koma Ahiya sanatha kupenya, popeza maso ace anali tong'o, cifukwa ca ukalamba wace.

5. Ndipo Yehova ananena ndi Ahiya, Taona, mkazi wa Yerobiamu akudza kukufunsa za mwana wace, popeza adwala; udzanena naye mwakuti mwakuti; popeza kudzakhala pakulowa iye adzadzizimbaitsa.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 14