Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 13:24-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Ndipo atacoka iye, mkango unakomana naye panjira, numupha, ndipo mtembo wace unagwera m'njiramo, buru naima pafupi, mkangonso unaima pafupi ndi mtembo.

25. Ndipo onani, anthu anapitapo naona mtembo wogwera m'njiramo, ndi mkango uli ciimire pafupi ndi mtembo, nadzanena m'mudzi m'mene munakhala mneneri wokalamba uja.

26. Ndipo mneneri amene uja anambweza panjirayo atamva, anati, Ndiye munthu uja wa Mulungu amene sanamvera mau a Yehova; cifukwa cace Yehova wampereka kwa mkango, numkadzula numupha, monga mwa mau a Yehova analankhula nayewo.

27. Iye nanena ndi ana ace, nati, Ndimangireni mbereko pa buru. Namangira mbereko.

28. Namuka iye, napeza mtembo wace wogwera m'njira, ndi buru ndi mkango ziti ciimire pafupi ndi mtembo. Mkango udalibe kudya mtembo, kapena kukadzula buru.

29. Ndipo mneneri ananvamula mtembo wa munthu wa Mulunguyo, nausenza pa buru, nabwera nao, nalowa m'mudzi mneneri wokalamba kumlira ndi kumuika.

30. Ndipo mtembo wace anauika m'manda a iye mwini, namlira iwo maliro, nati, Mayo, mbale wanga!

31. Ndipo kunacitika, atamuika iye, ananena ndi ana ace, nati, Nkadzamwalira ine mudzandiike ine m'manda momwemo mwaikidwa munthu wa Mulunguyo, ikani mafupa anga pafupi ndi mafupa ace.

32. Popeza mau aja anawapfuula mwa mau a Yehova kutemberera guwa la nsembe la ku Beteli, ndi kutemberera nyumba zonse za misanje iri m'midzi ya ku Samariya, adzacitika ndithu.

33. Pambuyo pa ici Yerobiamu sanabwerera pa njira yace yoipa, koma analonganso anthu acabe akhale ansembe a misanje, yensewakufuna yemweyu anampatula akhale wansembe wa misanje,

34. Ndimo umu munali chimo la nyumba ya Yerobiamu, limene linaidula ndi kuiononga pa dziko lapansi.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 13