Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 13:12-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Ndipo atate wao anati kwa iwo, Wapitira njira yiti? popeza ana ace adaona njira analowera munthu wa Mulungu anacokera ku Yudayo.

13. Nanena ndi ana ace, Ndimangireni mbereko pa buru. Namangira iwo mbereko pa buru, naberekekapo iye.

14. Natsata munthu wa Mulungu, nampeza ali, tsonga patsinde pa mtengo wathundu, nanena naye, Kodi ndiwe munthu wa Mulungu amene uja anacokera ku Yuda? Nati, Ndine amene.

15. Tsono ananena naye, Tiye kwathu, ukadye mkate.

16. Nan iye, Sindingabwerere nawe kukalowa kwanu, kapena kudya mkate, kapena kumwa nawe madzi pano;

17. pakuti mau a Yehova anadza kwa ine, nati Usakadye mkate, kapena kumwa madzi kumeneko, kapena kubwerera njira yomweyo unadzerayo.

18. Ndipo anati kwa iye, Inenso ndine mneneri wonga iwe, ndipo mthenga analankhula ndi ine mwa mau a Yehova, nati, Kambwezere kwanu, kuti akadye mkate, namwe madzi. Koma anamnamiza.

19. Tsono anabwerera naye, nakadya kwao, namwa madzi.

20. Ndipo kunacitika iwo ali cikhalire pagome, mau a Yehova anadza kwa mneneri amene anambwezayo,

21. napfuula iye kwa munthu uja wa Mulungu anacokera ku Yudayo, nati, Atero Yehova, Pokhala sunamvera mau a pakamwa pa Yehova, osasunga lamulo lija Yehova Mulungu wako anakulamulira,

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 13