Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 12:19-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Motero Aisrayeli anapandukana ndi nyumba ya Davide kufikira lero.

20. Ndipo kunali, atamva Aisrayeli onse kuti Yerobiamu wabweranso, anatuma kumuitanira iye kumsonkhano, namlonga iye mfumu ya Aisrayeli onse; palibe munthu anatsata nyumba ya Davide koma pfuko lokha la Yuda.

21. Ndipo Rehabiamu anafika ku Yerusalemu, nasonkhanitsa nyumba yonse ya Yuda, ndi pfuko la Benjamini, ankhondo osankhika zikwi zana limodzi mphambu makumi asanu ndi atatu, kuyambana nayo nyumba ya Israyeli, kubwezanso ufumu kwa Rehabiamu mwana wa Solomo.

22. Ndipo mau a Mulungu anafika kwa Semaya mneneri wa Mulungu, nati,

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 12