Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 11:8-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Ndipo momwemo anacitiranso akazi ace onse acilendo, amene amafukizira naphera nsembe mafano ao.

9. Ndipo Yehova anakwiya ndi Solomo, pokhala mtima wace unapambuka kwa Yehova Mulungu wa Israyeli, amene adamuonekera kawiri,

10. namlamulira za cinthu comweci, kuti asatsate milungu yina; koma iye sanasunga cimene Yehova anacilamula.

11. Cifukwa cace Yehova ananena ndi Solomo, Popeza cinthu ici cacitika ndi iwe, ndipo sunasunga cipangano canga ndi malemba anga amene ndinakulamulira, zedi, ndidzakung'ambira ufumu ndi kuupatsa mnyamata wako.

12. Koma m'masiku ako sindidzatero cifukwa ca Davide atate wako, koma ndidzaung'ambira m'manja mwa mwana wako;

13. komatu sindidzacotsa ufumu wonsewo; pfuko limodzi ndidzapatsa mwana wako, cifukwa ca Davide mtumiki wanga, ndi cifukwa ca Yerusalemu amene ndinamsankha.

14. Ndipo Yehova anamuutsira Solomo mdani, ndiye Hadadi M-edomu; iyeyo anali wa mbumba ya mfumu ya ku Edomu.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 11