21. Koma iye anayankha, nati kwa iwo, Amai wanga ndi abale anga ndiwo amene akumva mau a Mulungu, nawacita.
22. Ndipo panali limodzi la masiku aja, iye analowa m'ngalawa, ndi ophunzira ace; nati kwa iwo, Tiolokere ku tsidya lija la nyanja; ndipo anakankhiramo.
23. Ndipo m'mene iwo anali kupita pamadzi, iye anagona tulo, Ndipo panyanja panatsikira namondwe wa mphepo; ndipo podzala ndi madzi, analimkuopsedwa.
24. Ndipo anadza kwa iye, namuutsa, nanena, Ambuye, Ambuye, titayika, Ndipo anauka, nadzudzula mphepo ndi mafunde ace a madzi; pomwepo zinaleka, ndipo panagwa batao