4. Ndipo wacitatu anatsanulira mbale yace ku mitsinje ndi akasupe a madzi; ndipo kunasanduka mwazi.
5. Ndipo ndinamva mngelo wa madziwo nanena, Muli wolungama, amene muli, nimunali, Woyera Inu, cifukwa mudaweruza kotero;
6. popeza anatsanulira mwazi wa oyera mtima, ndi wa aneneri, ndipo mudawapatsa mwazi amwe; ayenera iwo.
7. Ndipo ndinamva wa pa guwa la nsembe, alinkunena, Inde, Ambuye Mulungu, Wamphamvuyonse, maweruziro anu ali oona ndi olungama.
8. Ndipo wacinai anatsanulira mbale yace padzuwa; ndipo analipatsa ilo litenthe anthu ndi moto.
9. Ndipo anatenthedwa anthu ndi kutentha kwakukuru; ndipo anacitira mwano dzina la Mulungu wokhala nao ulamuliro pa miliri iyi; ndipo sanalapa kuti amcitire ulemu.
10. Ndipo wacisanu anatsanulira mbale yace pa mpando wacifumu wa cirombo; ndipo ufumu wace unadetsedwa; ndipo anatafuna malilime ao ndi kuwawa kwace,