15. Ndipo inalabvulira m'kamwa mwace, potsata mkazi, madzi ngati mtsinje, kuti akakokoleredwe mkazi nao.
16. Ndipo dziko linathandiza mkaziyo, ndi dziko linatsegula m'kamwa mwace, nilinameza madzi a mtsinje amene cinjoka cinalabvula m'kamwamwace.
17. Ndipo cinjoka cinakwiya ndi mkazi, nicinacoka kunka kucita nkhondondi otsala ambeu yace, amene asunga malamulo a Mulungu, nakhala nao umboni wa Yesu.