45. ndi Yehudi, ndi Bene-beraki, ndi Gatirimoni;
46. ndi Me-jarikoni, ndi Rakoni, ndi malire pandunji pajapo.
47. Koma malire a ana a Dani anaturuka kupitirira iwowa; pakuti ana a Dani anakwera nathira nkhondo ku Lesemu, naulanda naukantha ndi lupanga lakuthwa, naulandira, nakhala m'mwemo, naucha Lesemu, Dani; ndilo dzina la Dani atate wao.
48. Ici ndi colowa ca pfuko la ana a Dani, monga mwa mabanja ao, midzi iyi ndi miraga yao.