39. Ici ndi colowa ca pfuko la ana a Nafitali, monga mwa mabanja ao, midzi ndi miraga yao.
40. Maere acisanu ndi ciwiri anaturukira pfuko la ana a Dani, monga mwa mabanja ao.
41. Ndipo malire a colowa cao anali Zora, ndi Esitaoli ndi Iri-semesi;
42. Saalabini, ndi Aijaloni ndi ltila;
43. ndi Eloni ndi Timna ndi Ekroni;
44. ndi Eliteke, ndi Gibetoni, ndi Baalati;
45. ndi Yehudi, ndi Bene-beraki, ndi Gatirimoni;
46. ndi Me-jarikoni, ndi Rakoni, ndi malire pandunji pajapo.
47. Koma malire a ana a Dani anaturuka kupitirira iwowa; pakuti ana a Dani anakwera nathira nkhondo ku Lesemu, naulanda naukantha ndi lupanga lakuthwa, naulandira, nakhala m'mwemo, naucha Lesemu, Dani; ndilo dzina la Dani atate wao.
48. Ici ndi colowa ca pfuko la ana a Dani, monga mwa mabanja ao, midzi iyi ndi miraga yao.
49. Ndipo atatha kuligawa dziko likhale colowa cao monga mwa malire ace, ana a Israyeli anapatsa Yoswa mwana wa Nuni colowa pakati pao;