33. Ndipo malire ao anayambira ku Helefi, ku thundu wa ku Zaanani, ndi Adaminekebi, ndi Yabineeli, mpaka ku Lakumu; ndi maturukiro ace anali ku Yordano;
34. nazungulira malire kumka kumadzulo ku Azinotu-tabori, naturukira komweko kumka ku Hukoku; nafikira ku Zebuloni kumwera, nafikira ku Aseri kumadzulo, ndi ku Yuda pa Yordano kum'mawa.
35. Ndipo midzi yamalinga ndiyo Zidimu, Zeri, ndi Hamati, Rakati, ndi Kinereti;
36. ndi Adama, ndi Rama, ndi Hazori;
37. ndi Kedesi, ndi Edrei, ndi Eni-hazori;
38. ndi Ironi, ndi Migidala-eli, Horemu, ndi Betianati, ndi Beti-semesi; midzi khumi ndi isanu ndi inai, ndi miraga yao.
39. Ici ndi colowa ca pfuko la ana a Nafitali, monga mwa mabanja ao, midzi ndi miraga yao.
40. Maere acisanu ndi ciwiri anaturukira pfuko la ana a Dani, monga mwa mabanja ao.
41. Ndipo malire a colowa cao anali Zora, ndi Esitaoli ndi Iri-semesi;
42. Saalabini, ndi Aijaloni ndi ltila;
43. ndi Eloni ndi Timna ndi Ekroni;
44. ndi Eliteke, ndi Gibetoni, ndi Baalati;
45. ndi Yehudi, ndi Bene-beraki, ndi Gatirimoni;
46. ndi Me-jarikoni, ndi Rakoni, ndi malire pandunji pajapo.