45. Ekroni pamodzi ndi midzi yace ndi miraga yao;
46. kuyambira ku Ekroni mpaka kunyanja, yonse ya ku mbali ya Asidodo, pamodzi ndi miraga yao.
47. Asidodo, midzi yace ndi miraga yace; Gaza, midzi yace ndi miraga yace; mpaka mtsinje wa Aigupto, ndi nyanja yaikuru ndi malire ace.
48. Ndi kumapiri Samiri, ndi Yatiri, om Soko;
49. ndi Dana, ndi Kiriyatisana, ndiwo Dibiri;
50. ndi Anabi, ndi Esitemo, ndi Animu;
51. ndi Goseni, ndi Holoni, ndi Gilo; midzi khumi ndi umodzi pamodzi ndi miraga yao.
52. Arabu, ndi Duma, ndi Esana;
53. ndi Yanimu, ndi Beti-tapua, ndi Apeka;
54. ndi Humita, ndi Kiriyatiariba, ndiwo Hebroni, ndi Ziori; midzi isanu ndi inai pamodzi ndi miraga yao.
55. Maoni, Karimeli, ndi Zifu, ndi Yuta;
56. ndi Yesireeli, ndi Yokideamu, ndi Zoona;
57. Kaini, Gibea ndi Timina; midzi khumi pamodzi ndi miraga yao.
58. Haluli, Beti-zuru, ndi Gedori,
59. ndi Maaratu, ndi Bete-anotu, ndi Elitekoni; midzi isanu ndi umodzi pamodzi ndi miraga yao.
60. Kiriyata-Baala, ndiwo KiriyatiYearimu ndi Raba; midzi iwiri pamodzi ndi miraga yao.
61. M'cipululu, Beti-araba, Midini, ndi Sekaka;
62. ndi Nibisani, ndi Mudzi wa Mcere, ndi En-gedi; midzi isanu ndi umodzi pamodzi ndi miraga yao.
63. Koma ana a Yuda sanakhoza kuingitsa Ayebusi, nzika za Yerusalemu: m'mwemo Ayebusi anakhala pamodzi ndi ana a Yuda, ku Yerusalemu, mpaka lero lino.