16. Ndipo Kalebe anati, iye amene akantha Kiriyati-Seferi, naulanda, yemweyo ndidzampatsa Akisa mwana wanga akhale mkazi wace.
17. Ndipo Otiniyeli mwana wa Kenazi, mbale wace wa Kalebe, anaulanda; ndipo anampatsa Akisa mwana wace akhale mkazi wace.
18. Ndipo kunali, m'mene anamdzera, anamkangamiza mwamuna wace kuti apemphe atate wace ampatse munda; ndipo anatsika pa buru; pamenepo Kalebe ananena naye, Ufunanji?
19. Nati iye, Mundipatse dalitso; popeza mwandipatsa dziko la kumwela, ndipatseninso zitsime za madzi. Pamenepo anampatsa zitsime za kumtunda, ndi zitsime za kunsi.
20. Ici ndi colowa ca pfuko la ana a Yuda monga mwa mabanja ao.
21. Ndipo midzi ya ku malekezero a pfuko la ana a Yuda ku malire a Edomu, kumwela ndiwo, Kabizeeli ndi Ederi, ndi Yaguri;
22. ndi Kina ndi Dimona, ndi Adada;
23. ndi Kedesi, ndi Hazori, ndi ltinani;
24. Zifi ndi Telemu ndi Bealoti;
25. ndi Hazorihadata, ndi Kerioti-hezirondi, ndiwo Hazori;
26. Amamu ndi Sema ndi Moloda;
27. ndi Hazara-gada, ndi Hesimoni, ndi Beti-peleti;
28. ndi Hazara-suala, ndi Beereseba, ndi Bizioti;
29. Baala, ndi lyimu, ndi Ezemu;
30. ndi Elitoladi, ndi Kesili ndi Horima;
31. ndi Zikilaga, ndi Madimana ndi Sanasana;
32. ndi Lebaoti, ndi Siliimu, ndi Aini ndi Rimoni; midzi yonse ndiyo makumi awiri kudza isanu ndi inai; pamodzi ndi miraga yao.