22. Cifukwa cace Yehova amene anaombola Abrahamu, atero za banja la Yakobo: Yakobo sadzakhala ndi manyazi tsopano, ngakhale nkhope yace tsopano sidzagwa.
23. Koma pamene iye aona ana ace, nchito ya manja anga, pakati pa iye, iwo adzayeretsa dzina langa; inde, iwo adzayeretsa Woyera wa Yakobo, nadzaopa Mulungu wa Israyeli.
24. Iwonso osocera mumzimu adzadziwa luntha, ndi iwo amene ang'ung'udza adzaphunzitsidwa.