6. Ukhala pakati pa manyengo m'manyengo; akana kundidziwa, ati Yehova.
7. Cifukwa cace atero Yehova wa makamu, Taonani, ndidzawasungunula, ndi kuwayesa, pakuti ndidzacitanji, cifukwa ca mwana wamkazi wa anthu anga?
8. Lilime lao ndi mubvi wakuphera; linena manyengo; wina anena mtendere ndi mnansi wace pakamwa pace, koma m'mtima mwace amlalira.
9. Kodi sindidzawalanga cifukwa ca izi? ati Yehova; kodi moyo wanga sudzabwezera cilango mtundu wotere?
10. Cifukwa ca mapiri ndidzagwa misozi ndi kulira, cifukwa ca mabusa a cipululu ndidzacita maliro, cifukwa apserera, kuti anthu sangathe kupitirirapo; ndiponso anthu sangathe kumva mau a ng'ombe zao; mbalame za mlengalenga ndi nyama zathawa, zapita.
11. Ndipo ndidzayesa Yerusalemu miyulu, mbuto ya ankhandwe; ndipo ndidzayesa midzi ya Yuda bwinja, lopanda wokhalamo.