27. Ndipo tsopano, walekeranji kumdzudzula Yeremiya wa ku Anatoti, amene amadziyesa mneneri wanu,
28. popeza watitumizira mau ku Babulo, akuti, Undende udzakhalitsa; mangani nyumba, khalani m'menemo; limani minda, idyani zipatso zao?
29. Ndipo Zefaniya wansembe anawerenga kalata amene m'makutu a Yeremiya mneneri.
30. Ndipo anadza mau a Yehova kwa Yeremiya, akuti,
31. Uwatumizire mau am'nsinga onse, akuti, Atero Yehova za Semaya Mnehelamu: Cifukwa Semaya wanenera kwa inu, koma Ine sindinamtuma, ndipo anakukhulupiritsani zonama;
32. cifukwa cace atero Yehova, Taonani, ndidzalanga Semaya Mnehelamu, ndi mbeu zace; sadzakhala ndi munthu wakukhala mwa anthu awa, sadzaona za bwino ndidzacitira anthu anga, ati Yehova: cifukwa wanena zopikisana ndi Yehova.