25. Iwo ndiwo mabanja a Isakara monga mwa owerengedwa ao; zikwi makumi asanu ndi limodzi mphambu zinai kudza mazana atatu.
26. Ana amuna a Zebuloni monga mwa mabanja ao ndiwo: Seredi, ndiye kholo la banja la Aseredi; Eloni, ndiye kholo la banja la Aeloni; Yahaliyeli, ndiye kholo la banja la Ayahaliyeli.
27. Iwo ndiwo mabanja a Zebuloni monga mwa owerengedwa ao, zikwi makumi asanu ndi limodzi mphambu mazana asanu.
28. Ana amuna a Yosefe monga mwa mabanja ao ndiwo: Manase ndi Efraimu.
29. Ana a Manase ndiwo: Makiri, ndiye kholo la banja la Amakiri; ndipo Makiri anabala Gileadi; ndiye kholo la banja la Agileadi,
30. Ana a Gileadi ndiwo: Yezeri, ndiye kholo la banja la Ayezeri; Heleki, ndiye kholo la banja la Aheleki;
31. ndi Asiriyeli, ndiye kholo la banja la Aasiriyeli; ndi Sekemu, ndiye kholo la banja la Asekemu;
32. ndi Semida, ndiye kholo la banja la Asemida; ndi Heferi, ndiye kholo la banja la Aheferi.
33. Ndipo Tselofekadi mwana wa Heferi analibe ana amuna, koma ana akazi ndiwo; ndipo maina a ana akazi a Tselofekadi ndiwo Mala ndi Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza.
34. Iwo ndiwo mabanja ao a Manase; ndipo owerengedwa ao ndiwo zikwi makumi asanu mphambu ziwiri kudza mazana asanu ndi awiri.
35. Ana amuna a Efraimu monga mwa mabanja ao ndiwo: Sutela, ndiye kholo la banja la Asutela; Bekeri, ndiye kholo la banja la Abekeri; Tahana, ndiye kholo la banja la Atahana.
36. Ndipo mwana wamwamuna wa Sutela ndiye Erani, ndiye kholo la banja la Aerani.
37. Iwo ndiwo mabanja a ana a Efraimu monga mwa owerengedwa ao, ndiwo zikwi makumi atatu mphambu ziwiri kudza mazana asanu. Iwo ndiwo ana amuna a Yosefe monga mwa mabanja ao.