10. Momwemo tsiku lakukondwera inu, ndi nyengo zoikidwa zanu, ndi poyamba miyezi yanu, muziliza malipenga pa nsembe zanu zopsereza, ndi pa nsembe zanu zoyamika; ndipo akhale kwa inu cikumbutso pamaso pa Mulungu wanu; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
11. Ndipo kunacitika, caka caciwiri, mwezi waciwiri, tsiku la makumi awiri la mweziwo, kuti mtambo unakwera kucokera kwa kacisi wa mboni.
12. Ndipo ana a Israyeli anayenda monga mwa maulendo ao, kucokera m'cipululu ca Sinai; ndi mtambo unakhala m'cipululu ca Parana.
13. Potero anayamba ulendo wao monga mwa mau a Yehova ndi dzanja la Mose.
14. Ndipo anayamba kuyenda a mbendera ya cigono ca ana a Yuda monga mwa magulu ao; woyang'anira gulu lace ndiye Nahesoni mwana wa Aminadabu.
15. Ndi pa gulu la pfuko la ana a Isakara panali Netaneli mwana wa Zuwara.
16. Ndi pa gulu la pfuko la ana a Zebuloni panali Eliyabu mwana wa Heloni.
17. Ndipo anagwetsa kacisi; ndi ana a Gerisoni, ndi ana a Merari, akunyamula kacisi, anamuka naye.
18. Ndi a mbendera ya cigono ca Rubeni, anayenda monga mwa magulu ao; ndipo pa gulu lace anayang'anira Elizuri mwana wa Sedeuri.
19. Ndi pa gulu la pfuko la ana a Simeoni anayang'anira Selumiyeli mwana wa Zurisadai.
20. Ndi pa gulu la pfuko la ana a Gadi anayang'anira Eliyasafe mwana wa Deyueli.
21. Pamenepo Akohati anayenda, ndi kunyamula zopatulika, ndi enawo anautsiratu kacisi asanafike iwowa.
22. Ndipo anayenda a mbendera ya cigono ca ana a Efraimu, monga mwa magulu ao; ndi pa gulu lace anayang'anira Elizama mwana wa Amihudi.
23. Ndi pa gulu la pfuko la ana a Manase anayang'anira Gamaliyeli mwana wa Pedazuri.
24. Ndi pa gulu la pfuko la ana a Benjamini anayang'anira Abidana mwana wa Gideoni.